Psalms 96

1Imbirani Yehova nyimbo yatsopano;
Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
2Imbirani Yehova, tamandani dzina lake;
lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
3Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko,
ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.

4Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda;
ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
5Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano,
koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
6Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake,
mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.

7Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina,
perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
8Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake;
bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
9Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake;
njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.

10Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.”
Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe;
Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
11Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere;
nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
12minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo.
Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
13idzayimba pamaso pa Yehova,
pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi;
adzaweruza dziko lonse mwachilungamo
ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.
Copyright information for NyaCCL